Malemba Opatulika

Malemba Opatulika The is the God page

09/02/2026

Mzimu oyera atifungatile mu Usiku umeneu Amen

08/02/2026

*KUVOMEREZANA NAYE MULUNGU*
Masalmo 133:1,3
1. Onani, nkokoma ndi kokondweretsa ndithu Kuti abale akhale pamodzi! 3. Ngati mame a ku Hermoni, Akutsikira pa mapiri a Ziyoni: Pakuti pamenepo Yehova analamulira dalitsolo, Ndilo moyo womka muyaya.
✅Mulungu akukondwera kuti ife okhulupilira tizikhalira pamodzi
✅Pamodzi mu pemphero,mu Uzimu,Mu chiyanjano,mu chilimbikitso,mu chikondi,mu chiphunzitso!
✅Mu umodzi timaonetsera chimene Mulungu ali....si Mulungu wa magawano/mipatiko ai.
✅Umodzi wa chikhulupiliro timalemekezana ndikukondana kweni-kweni
✅Pamene tili pamodzi mu thupi timakhalaso pamodzi mu uzimu mwathu!
✅Mulungu akaona umodzi wathu sakhala chete koma kulamulirapo dalitso ndilo moyo omka muyaya.
_MULUNGU ALI MU NTCHITO YOLIMBIKITSA UMODZI_
❌Pamene ndayamba kuganiza zoipa za munthu yemwe Mulungu wandiyanjanitsa ku uzimu ndimakhala ndasiyana naye Mulungu .
❌Zoonadi pamene NDIKUGANIZA zolimbana Ndi anthu omwe akhala akusiya zawo mkumaima nane kuti ndipambane apa ndimakhala ndikudziononga
*ZOLINGA ZA MULUNGU PA INU ZIPOSA ZOFUNA ZANU*
👌Mulungu sanagonjeko ku zofuna za anthu mkale lonse! Koma Ndi anthu omwe amagonja. Ngakhale tilimbane Ndi zomwe Mulungu akufuna pa ife zimangotitengera kuonongeka kwa zinthu zathu chifukwa zomwe Mulungu akufuna zimachitika ndithu
👌Mulungu sali monga munthu kuti akhoza kuvomera chilichonse chomwe taganiza kuti tichite....chifukwa zambiri zomwe timaziona ngati zitipatsa tsogolo Mulungu amakhala asakuonamo tsogolo,nchifukwa chake amatiletsa!
👌Maso athu nthawi zambiri amaona za apa pomwe Mulungu amaona za uko! Ndie nchifukwa chake tisanachite kalikose timayenera timufuse odziwa za uko ativomereze pa zomwe tikufuna kuchitazo.
✅"Akapanda kumanga nyumba Yehova,akuimanga aimanga chabe"(masalimo 127:1)Ngati si Mulungu akukutsogolerani pa zomwe mukufuna kuchitazo dziwani zikhala za chabe!
✅Zikufunika azikhala Mulungu pachiyambi cha ma plan athu. Ndipo zizithera Mulungu. Mamawa Wabwino

07/02/2026

Masalimo 23:1- amati chani?
Mawa tikuphuzitsana za chapter chimenechi Amen

08/08/2025

Moyo ukuyenda bwanji abale ndi alongo konse muli? ife kuno za mphavu kwambili

02/08/2025

Masalimo 34 vs 9
Opani Yehova, inu oyera ake, pakuti onse omuopa sasowa kanthu Amen.
ngati tiopa Yehova akuti sitidzasowa kanthu

30/01/2025

Tiyamike Mulungu potidzutsa ndi moyo wathazi komanso kuti tagwila ntchito zosiyanasiyana, ma business ndizina zotelo kufikila madzulo ano tikugona pamene ena ali pa ulendo ena kugwila ntchito kumene, tipempha madalitso komanso chitetezo zitifungatile kuti mawa tidzukenso ndi moyo wanthazi, Amen

19/01/2025

Moyo wanu ukuyenda bwanji konse muli? Ife kuno Ambue akutisamala

27/10/2024

Mwawela bwanji kose komwe muli?

25/07/2023

Zikomo Mulungu wathu chifukwa cha mphatso ya moyo mwatidzutsa nao lero, Amen.

22/06/2022

Good morning people . thanks to God that we are okay

30/05/2022

Mwazuka bwanji abale ndi alongo nonse mwa Ambuye? Nkutheka kuti tili m'magulu osiyana siyana Kaya ndipa WhatsApp ndafuna ndikudziwitseni kuti munthune ndataya wallet ku area 28 kanengo muli Driving license, Identity card ndi ndalama, ndizotheka kuti mwina ena aponyako m'ma group kuti watola wallet muli driving license yolemba James Tanganyika, mukavelako number ndi iyi 0995896789 call or WhatsApp please. Mukhale ndi tsiku lopambana

Address

Likuni

Telephone

+265882166178

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Malemba Opatulika posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Malemba Opatulika:

Share

Category