15/01/2026
tamvani nkhani yanga komanso ngati mkontheka ena aziwitseniko.
Dzina langa ndiine...dzaka zanga zakubadwa 28,ndakula moyo ovutika kuti ndimalidze mamphuziro anga asekondale sizinali zomphweka,ndinadalitsika ndi lunso lamaimbidwe koma ndalama yopitira ku studio inali yondivuta kufikira pomwe mzanga wina anandiuza kuti akukajambula nyimbo ndipo ndimupelekedze.tinafika ku studio anayambapo kuimba mwina ndi mwina zimamuvuta ndipo ndinayamba kumuwunikira zomwe zinapangitsa kuti adipose mpata oimba komatu ndinaswa nyimbo ngati yanga zomwe olo ojambula zinamupasa chidwi.(fast forward)
ndinalandira unthenga kuti ndikufunika ku studio kuja nditafika ndinapedza oimba wina oziwika bwino komanso manager wake ndipo ojambula anati man takulandirani ndimakoza koza nyimbo yanu ndipo mabwanawa atamva mawu anu zawasangalatsa kotero akufuna akuloweseni mu gulu lawo,anandiuza zonse zofunika ndipo nyimbo ndinayamba kujambula ndinatchuka mukanthawi kochepa moti anthu ambiri otchuka anakhala amzanga ndalama inayamba kupedzeka moyo unasintha olo kwanthu anthu amamva kukoma,tsiku lina tinapita ku shire highlands kukaimba itantha show anati tonse tigona mkokuno kukubwera azungu amene akufuna andione mwapadera ndiomba azanga.
manager analakhula Modenkha enanu mukuziwa kale zochita,ananditengela ku room yomwe anati ndigona ndipo anati man lija ndikale munyamba kuimba nthawi yakwana kuti inunso mukhale ngati amzanuwa taonani muli gulu limodzi komano inuyo Galimoto olo nyumba mulibe,ndiye azungu omwe akubwerawa ndiwo eni Label yanthuyi ndiye ndizosavuta inuyo mungogona nawo basi mukatero ndiinu millionaire ndipo olo kunja ma show muzikaimba sinatekeseke pansi pa mtima ndinanyadira ndani safuna kugona ndi mzungu chosaziwa anali azimbambo okha okha ndipo anali owoti andigona ineyo.mmmmh ndinachita tsemwe anandiuza ngati sindilola ndisauka nyimbo zanga zilowa pansi kumbukirani kuti kangachepe komwe ndimapedza kamanthandiza azibale komanso makolo ndipo apa ndilemela kwambiri akandigona,chifukwa choopa kubwelera moyo wawumphawu ndinalolera ndipo moyo wanga unasinthiratu pano chilichose ndili nacho ndipo moyo ukufewa kunkhani yazachuma komano munthune ndatopa nalo nkhalidweli ndikufuna nditasiya chifukwa izi zimachitika kawiri kawiri maka album iliyonse isanatuluke timayenela kugonedwa ndinthu koma apa ndikufuna kusiya koma ndikuopa kuti chuma changa sichitintha?lunso langa sililowa pansi?kunena zoona ndabalalika chonde ndinthandizeni ndiyambire pati chifukwa moyo wawumphawi ndiye sindikuufunanso komanso kupembeza mafanowa sindikufuna ndikufuna moyo wa mtendere.